Sunday, April 28, 2024

A Billy Malata awona nyekhwe khoti litawatumiza ku ndende ya Maula poipitsa mbiri ya a ena pogwiritsa ntchito masamba a mchezo

Must Read

Bwalo la milandu laling’ono ku Nathenje, latumiza mkulu woyang’anira nkhani za ndale m’chipani cha DPP, a Fredrick Billy Malata ku ndende ya Maula kwa masiku asanu ndi awiri (7).

A Malata, adamangidwa loweruka pa mlandu woipitsa mbiri ya wochita malonda a Alfred Gangata pogwiritsa ntchito masamba a mchezo.

Iwo adatengeredwa ku bwalo la milandu ku Nathenje dzulo ndipo bwalo lawatumiza ku Maula kwa amasiku 7 ponena kuti chigamulo pa pempho lawo la belo chidzapelekedwa Lachiwiri sabata ya mawa.

Owayimilira a Malata a Gladwell Majekete atsimikiza za izi ndipo ati a Malata akasiyidwa ku Maula m’mawa wa lero atagona usiku wadzulo ku polisi ya Nathenje.

Akulowa ku ndende ya Maula, a Malata adalankhura mwachidule ndi Times 360 Malawi ndipo anati: “Amalawi akufuna kwabwino andithandize. Ombudsman, a Chief Justice komanso Inspector General of police andithandize ndikuvutika. Ndagona ku Area 3 police masiku atatu, dzulo ndagona ku Nathenje lero akukandisiya ku Maula pa nkhani zosamveka. Panopa mu zovala zanga muli msikidzi zokhazokha, ndikuvutika.”

- Advertisement -spot_img

LEAVE A REPLY

Please enter your comment!
Please enter your name here

- Advertisement -spot_img
Latest News

Tonse Alliance government has abandoned Malawians- Chihana speaks out

Ahead of the Labour Day rally, dubbed "Agricultural sector catalyst for stable democracy and socioeconomic transformation" the Alliance for...
- Advertisement -spot_img

More Articles Like This

- Advertisement -spot_img