Saturday, July 27, 2024

A Billy Malata awona nyekhwe khoti litawatumiza ku ndende ya Maula poipitsa mbiri ya a ena pogwiritsa ntchito masamba a mchezo

Must Read

Bwalo la milandu laling’ono ku Nathenje, latumiza mkulu woyang’anira nkhani za ndale m’chipani cha DPP, a Fredrick Billy Malata ku ndende ya Maula kwa masiku asanu ndi awiri (7).

A Malata, adamangidwa loweruka pa mlandu woipitsa mbiri ya wochita malonda a Alfred Gangata pogwiritsa ntchito masamba a mchezo.

Iwo adatengeredwa ku bwalo la milandu ku Nathenje dzulo ndipo bwalo lawatumiza ku Maula kwa amasiku 7 ponena kuti chigamulo pa pempho lawo la belo chidzapelekedwa Lachiwiri sabata ya mawa.

Owayimilira a Malata a Gladwell Majekete atsimikiza za izi ndipo ati a Malata akasiyidwa ku Maula m’mawa wa lero atagona usiku wadzulo ku polisi ya Nathenje.

Akulowa ku ndende ya Maula, a Malata adalankhura mwachidule ndi Times 360 Malawi ndipo anati: “Amalawi akufuna kwabwino andithandize. Ombudsman, a Chief Justice komanso Inspector General of police andithandize ndikuvutika. Ndagona ku Area 3 police masiku atatu, dzulo ndagona ku Nathenje lero akukandisiya ku Maula pa nkhani zosamveka. Panopa mu zovala zanga muli msikidzi zokhazokha, ndikuvutika.”

- Advertisement -spot_img

LEAVE A REPLY

Please enter your comment!
Please enter your name here

- Advertisement -spot_img
Latest News

TNM gives Umthetho Festival K5M boost…Zulu nation King kaZwelithini coming

Lilongwe, July 25, 2024–In fostering cultural heritage and unity, TNM Plc, has contributed K5 million towards this year’s celebration...
- Advertisement -spot_img

More Articles Like This

- Advertisement -spot_img